Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 3:14-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Pamodzi ndi mafumu ndi maphungu a padziko,Akudzimangira m'mabwinja;

15. Kapena pamodzi ndi akalonga eni ace a golidi,Odzaza nyumba zao ndi siliva;

16. Kapena ngati nsenye yobisika ndikadakhala kuli zi;Ngati makanda osaona kuunika.

17. Apo oipa aleka kumabvuta;Ndi apo ofoka mphamvu akhala m'kupumula.

18. Apo a m'kaidi apumula pamodzi,Osamva mau a wofulumiza wao.

19. Ang'ono ndi akulu ali komwe;Ndi kapolo amasuka kwa mbuyace.

20. Amninkhiranji kuunika wobvutika,Ndi moyo kwa iye wakuwawa mtima,

21. Wakuyembekezera imfa, koma kuli zi,Ndi kuikumba koposa cuma cobisika,

22. Wakusekerera ndi cimwemweNdi kukondwera pakupeza manda?

23. Amuonetseranji kuunika munthu wa njira yobisika,Amene wamtsekera Mulungu?

Werengani mutu wathunthu Yobu 3