Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 3:1-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Atatero, Yobu anatsegula pakamwa pace, natemberera tsiku lace.

2. Nalankhula Yobu nati,

3. Litayike tsiku lobadwa ine,Ndi usikuwo udati, Waima naye mwana wamwamuna.

4. Tsiku lija likhale mdima;Mulungu asalifunse kumwamba,Ndi kuunika kusaliwalire.

5. Mdima ndi mthunzi wa imfa ziliyese lao lao;Mtambo ulikhalire;Zonse zodetsa usana bi ziliopse.

6. Usiku uja, mdima weni weni uugwere;Usakondwerere mwa masiku a m'caka;Usalowe m'ciwerengedwe ca miyezi.

7. Ha! usiku uja ukhale cumba;Kuyimbira kokondwera kusalowem'mwemo.

8. Autemberere iwo akutemberera usana,Odziwa kuutsa cinjokaco.

9. Nyenyezi za cizirezire zide;Uyembekezere kuunika, koma kuusowe;Usaone kuphenyuka kwa mbanda kuca;

10. Popeza sunatseka pa makomo ace mimba ya mai wanga.Kapena kundibisira mabvuto pamaso panga.

11. Ndinalekeranji kufera m'mimba?Ndi kupereka mzimu wanga pobadwa ine?

12. Anandilandiriranji maondo?Kapena mabere kuti ndiyamwe?

13. Pakuti ndikadagona pansi pomwepo ndi kukhala cete;Ndikanagona tulo; pamenepo ndikadaona popumula;

14. Pamodzi ndi mafumu ndi maphungu a padziko,Akudzimangira m'mabwinja;

15. Kapena pamodzi ndi akalonga eni ace a golidi,Odzaza nyumba zao ndi siliva;

Werengani mutu wathunthu Yobu 3