Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 29:7-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Muja ndinaturuka kumka kucipata kumudzi,Muja ndinakonza pokhala panga kukhwalala,

8. Anyamata anandiona nabisala,Okalamba anandinyamukira, nakhala ciriri,

9. Akalonga anadziletsa kulankhula,Ndi kugwira pakamwa pao;

10. Mau a omveka anali zi,Ndi lilime lao linamamatira ku malakalaka ao.

11. Pakuti pondimva ine khutu, linandidalitsa;Ndipo pondiona diso, linandicitira umboni.

12. Pakuti ndinapulumutsa wozunzika wakupfuula;Mwana wamasiye yemwe wosowa mthandizi.

13. Dalitso la iye akati atayike linandidzera,Ndi mtima wa mkazi wamasiye ndinauyimbitsa mokondwera.

14. Ndinabvala cilungamo, ndipo cinandibvala ine;Ciweruzo canga cinanga mwinjiro ndi nduwira.

15. Ndinali maso a akhungu,Ndi mapazi a otsimphina.

16. Ndinali atate wa waumphawi;Ndi mlandu wa iye amene sindinamdziwa ndinafunsitsa.

Werengani mutu wathunthu Yobu 29