18. Pamenepo ndinati, Ndidzatsirizika m'cisa canga;Ndipo ndidzacurukitsa masiku anga ngati mcenga.
19. Muzu wanga watambalala kufikira kumadzi;Ndi mame adzakhala pa nthambi yanga usiku wonse.
20. Ulemu wanga udzakhala wosaguga mwa ine,Ndi uta wanga udzakhala wosalifuka m'dzanja mwanga.
21. Anthu anandimvera, nalindira,Nakhala cete, kuti ndiwapangire.