Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 29:10-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Mau a omveka anali zi,Ndi lilime lao linamamatira ku malakalaka ao.

11. Pakuti pondimva ine khutu, linandidalitsa;Ndipo pondiona diso, linandicitira umboni.

12. Pakuti ndinapulumutsa wozunzika wakupfuula;Mwana wamasiye yemwe wosowa mthandizi.

13. Dalitso la iye akati atayike linandidzera,Ndi mtima wa mkazi wamasiye ndinauyimbitsa mokondwera.

14. Ndinabvala cilungamo, ndipo cinandibvala ine;Ciweruzo canga cinanga mwinjiro ndi nduwira.

15. Ndinali maso a akhungu,Ndi mapazi a otsimphina.

16. Ndinali atate wa waumphawi;Ndi mlandu wa iye amene sindinamdziwa ndinafunsitsa.

17. Ndipo ndinatyola nsagwada ya wosalungama,Ndi kukwatula cogwidwa kumano kwace.

18. Pamenepo ndinati, Ndidzatsirizika m'cisa canga;Ndipo ndidzacurukitsa masiku anga ngati mcenga.

19. Muzu wanga watambalala kufikira kumadzi;Ndi mame adzakhala pa nthambi yanga usiku wonse.

20. Ulemu wanga udzakhala wosaguga mwa ine,Ndi uta wanga udzakhala wosalifuka m'dzanja mwanga.

21. Anthu anandimvera, nalindira,Nakhala cete, kuti ndiwapangire.

Werengani mutu wathunthu Yobu 29