Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 29:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yobu anaonjezanso mwambi wace, nati,

2. Ha! ndikadakhala monga m'miyezi yapitayi,Monga m'masiku akundisunga Mulungu;

3. Muja nyali yace inawala pamutu panga,Ndipo ndi kuunika kwace ndinayenda mumdima;

4. Monga umo ndinakhala m'masiku anga olimba,Muja uphungu wa Mulungu unakhala pahema panga;

5. Muja Wamphamvuyonse akali nane pamodzi,Ndi ana anga anandizinga;

6. Muja popondera ine padakhatamira ndi mafuta amkaka,Ndi thanthwe linanditsanulira mitsinje ya mafuta aazitona!

7. Muja ndinaturuka kumka kucipata kumudzi,Muja ndinakonza pokhala panga kukhwalala,

8. Anyamata anandiona nabisala,Okalamba anandinyamukira, nakhala ciriri,

9. Akalonga anadziletsa kulankhula,Ndi kugwira pakamwa pao;

10. Mau a omveka anali zi,Ndi lilime lao linamamatira ku malakalaka ao.

11. Pakuti pondimva ine khutu, linandidalitsa;Ndipo pondiona diso, linandicitira umboni.

12. Pakuti ndinapulumutsa wozunzika wakupfuula;Mwana wamasiye yemwe wosowa mthandizi.

Werengani mutu wathunthu Yobu 29