Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 28:9-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Munthu atambasulira dzanja lace kumwala;Agubuduza mapiri kuyambira kumizu.

10. Asema njira pakati pa matanthwe,Ndi diso lace liona ciri conse ca mtengo wace.

11. Atseka mitsinje ingadonthe;Naturutsira poyera cobisikaci.

12. Koma nzeru, idzapezeka kuti?Ndi luntha, malo ace ali kuti?

13. Munthu sadziwa mtengo wace;Ndipo silipezeka m'dziko la amoyo.

14. Pozama pakuti, Mwa ine mulibe;Ndi nyanja ikuti, Kwa ine kulibe.

Werengani mutu wathunthu Yobu 28