Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 28:7-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Njira imeneyi palibe ciombankhanga ciidziwa;Lingakhale diso la kabawi losapenyapo.

8. Nyama zodzikuza sizinapondapo,Ngakhale mkango waukali sunapitapo.

9. Munthu atambasulira dzanja lace kumwala;Agubuduza mapiri kuyambira kumizu.

10. Asema njira pakati pa matanthwe,Ndi diso lace liona ciri conse ca mtengo wace.

11. Atseka mitsinje ingadonthe;Naturutsira poyera cobisikaci.

12. Koma nzeru, idzapezeka kuti?Ndi luntha, malo ace ali kuti?

13. Munthu sadziwa mtengo wace;Ndipo silipezeka m'dziko la amoyo.

Werengani mutu wathunthu Yobu 28