Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 28:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Miyala yace ndiyo malo a safiro,Ndipo iri nalo pfumbi lagolidi.

7. Njira imeneyi palibe ciombankhanga ciidziwa;Lingakhale diso la kabawi losapenyapo.

8. Nyama zodzikuza sizinapondapo,Ngakhale mkango waukali sunapitapo.

9. Munthu atambasulira dzanja lace kumwala;Agubuduza mapiri kuyambira kumizu.

10. Asema njira pakati pa matanthwe,Ndi diso lace liona ciri conse ca mtengo wace.

11. Atseka mitsinje ingadonthe;Naturutsira poyera cobisikaci.

Werengani mutu wathunthu Yobu 28