Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 28:15-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Silipezeka ndi golidi,Sayesapo siliva mtengo wace.

16. Sailinganiza ndi golidi wa Ofiri,Ndi sohamu wa mtengo wace wapatali kapena safiro.

17. Golidi ndi krustalo sizilingana nayo;Ndi kusinthana kwace, siisinthanika ndi zisambiro za golidi woyengetsa.

18. Korali kapena ngale sizikumbukikapo.Mtengo wace wa nzeru uposa wa korali wofiira.

19. Topazi wa Kusi sufanana nayo,Sailinganiza ndi golidi wolongosoka.

20. Koma nzeru ifuma kuti?Ndi luntha, pokhala pace pali kuti?

21. Popeza pabisikira maso a zamoyo zonse,Pabisikiranso mbalame za m'mlengalenga,

22. Cionongeko ndi Imfa zikuti,Tamva mbiri yace m'makutu mwathu.

23. Mulungu ndiye: azindikira njira yace,Ndiye adziwa pokhala pace.

24. Pakuti apenyerera malekezero a dziko lapansi,Naona pansi pa thambo ponse;

Werengani mutu wathunthu Yobu 28