Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 28:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Pozama pakuti, Mwa ine mulibe;Ndi nyanja ikuti, Kwa ine kulibe.

15. Silipezeka ndi golidi,Sayesapo siliva mtengo wace.

16. Sailinganiza ndi golidi wa Ofiri,Ndi sohamu wa mtengo wace wapatali kapena safiro.

17. Golidi ndi krustalo sizilingana nayo;Ndi kusinthana kwace, siisinthanika ndi zisambiro za golidi woyengetsa.

18. Korali kapena ngale sizikumbukikapo.Mtengo wace wa nzeru uposa wa korali wofiira.

19. Topazi wa Kusi sufanana nayo,Sailinganiza ndi golidi wolongosoka.

20. Koma nzeru ifuma kuti?Ndi luntha, pokhala pace pali kuti?

Werengani mutu wathunthu Yobu 28