17. Azikonzeretu, koma wolungama adzazibvala,Ndi wosalakwa adzagawa ndalamazo.
18. Amanga nyumba yace ngati kadzoce,Ndi ngati wolindira amanga dindiro.
19. Agona pansi ali wacuma, koma saikidwa;Potsegula maso ace, wafa cikomo,
20. Zoopsa zimgwera ngati madzi;Nkuntho umtenga usiku.
21. Mphepo ya kum'mawa Imtenga, nacokaiye;Nimkankha acoke m'malo mwace.
22. Pakuti Mulungu adzamponyera zoopsa, osanlieka;Kuthawa akadathawa m'dzanja lace.