Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 27:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Azikonzeretu, koma wolungama adzazibvala,Ndi wosalakwa adzagawa ndalamazo.

18. Amanga nyumba yace ngati kadzoce,Ndi ngati wolindira amanga dindiro.

19. Agona pansi ali wacuma, koma saikidwa;Potsegula maso ace, wafa cikomo,

20. Zoopsa zimgwera ngati madzi;Nkuntho umtenga usiku.

21. Mphepo ya kum'mawa Imtenga, nacokaiye;Nimkankha acoke m'malo mwace.

22. Pakuti Mulungu adzamponyera zoopsa, osanlieka;Kuthawa akadathawa m'dzanja lace.

Werengani mutu wathunthu Yobu 27