Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 27:14-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Akacuruka ana ace, ndiko kucurukira lupanga,Ndi ana ace sadzakhuta cakudya.

15. Akumtsalira iye adzaikidwa muimfa,Ndi akazi ace amasiye sadzalira maliro.

16. Cinkana akundika ndalama ngati pfumbi,Ndi kukonzeratu zobvala ngati dothi;

17. Azikonzeretu, koma wolungama adzazibvala,Ndi wosalakwa adzagawa ndalamazo.

18. Amanga nyumba yace ngati kadzoce,Ndi ngati wolindira amanga dindiro.

19. Agona pansi ali wacuma, koma saikidwa;Potsegula maso ace, wafa cikomo,

Werengani mutu wathunthu Yobu 27