Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 27:11-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndidzakulangizani za dzanja la Mulungu;Cokhala ndi Wamphamvuyonse sindidzacibisa.

12. Taonani, inu nonse munaciona;Ndipo mugwidwa nazo zopanda pace cifukwa ninji?

13. Ili ndi gawo la munthu woipa kwa Mulungu,Ndi colowa ca akupsinja anzao acilandira kwa Wamphamvtiyonse.

14. Akacuruka ana ace, ndiko kucurukira lupanga,Ndi ana ace sadzakhuta cakudya.

15. Akumtsalira iye adzaikidwa muimfa,Ndi akazi ace amasiye sadzalira maliro.

16. Cinkana akundika ndalama ngati pfumbi,Ndi kukonzeratu zobvala ngati dothi;

17. Azikonzeretu, koma wolungama adzazibvala,Ndi wosalakwa adzagawa ndalamazo.

18. Amanga nyumba yace ngati kadzoce,Ndi ngati wolindira amanga dindiro.

19. Agona pansi ali wacuma, koma saikidwa;Potsegula maso ace, wafa cikomo,

20. Zoopsa zimgwera ngati madzi;Nkuntho umtenga usiku.

21. Mphepo ya kum'mawa Imtenga, nacokaiye;Nimkankha acoke m'malo mwace.

22. Pakuti Mulungu adzamponyera zoopsa, osanlieka;Kuthawa akadathawa m'dzanja lace.

Werengani mutu wathunthu Yobu 27