Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 22:1-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha, nati,

2. Kodi munthu apindulira Mulungu?Koma wanzeru angodzipindulira yekha.

3. Kodi Wamphamvuyonse akondwera nako kuti iwe ndiwe wolungama?Kapena kodi apindula nako kuti ukwaniritsa njira zako?

4. Kodi akudzudzula, nadza nawe kumlandu,Cifukwa ca kumuopa kwako?

5. Zoipa zako sizicuruka kodi?Ndi mphulupulu zako sizikhala zosawerengeka kodi?

6. Pakuti wamtenga cikole kwa mbale wako wopanda cifukwa,Ndi kubvula ausiwa zobvala zao.

7. Sunampatsa wolema madzi amwe,Ndi wanjala unammana cakudya.

8. Koma munthu mwini mphamvu, dziko ndi lace;Ndi munthu wobvomerezeka, anakhala momwemo.

9. Unabweza akazi amasiye osawaninkha kanthu,Ndi manja a ana amasiye anatyoledwa.

10. Cifukwa cace misampha ikuzinga.Ndi mantha akubvuta modzidzimutsa,

11. Kapena mdima kuti ungaone,Ndi madzi aunyinji akumiza.

12. Kodi Mulungu sakhala m'mwamba m'tali?Ndipo penyani kutalika kwace kwa nyenyezi, ziri m'talitali.

13. Ndipo ukuti, Adziwa ciani Mulungu?Aweruza kodi mwa mdima wa bii?

Werengani mutu wathunthu Yobu 22