Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 21:9-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Nyumba zao sizitekeseka ndi mantha,Ngakhale ndodo ya Mulungu siiwakhalira.

10. Ng'ombe yao yamphongo imakwera, yosakanika;Ng'ombe yao yaikazi imaswa, yosapoloza.

11. Aturutsa makanda ao ngati gulu,Ndi ana ao amabvinabvina.

12. Ayimbira lingaka ndi zeze,Nakondwera pomveka citoliro.

13. Atsekereza masiku ao ndi zokoma,Natsikira m'kamphindi kumanda.

14. Koma adati kwa Mulungu, Ticokereni;Pakuti sitifuna kudziwa njira zanu.

15. Wamphamvuyonse ndiye yani kuti timtumikire?Ndipo tidzapindulanji pakumpemphera Iye?

16. Taonani, zokoma zao siziri m'dzanja lao;(Koma uphungu wa oipa unditalikira.)

Werengani mutu wathunthu Yobu 21