Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 21:24-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Mbale zace zidzala ndi mkaka;Ndi wongo wa m'mafupa ace uli momwe.

25. Koma mnzace akufa ali nao mtima wakuwawa,Osalawa cokoma konse.

26. Iwo agona cimodzimodzi kupfumbi,Ndi mphutsi ziwakuta.

27. Taonani, ndidziwa maganizo anu,Ndi ciwembu mundilingirira moipa,

28. Pakuti munena, Iri kuti nyumba ya kalonga?Ndi hema wokhalamo woipa ali kuti?

29. Simunawafunsa kodi opita m'njira?Ndipo simusamalira zotsimikiza zao?

Werengani mutu wathunthu Yobu 21