Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 21:15-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Wamphamvuyonse ndiye yani kuti timtumikire?Ndipo tidzapindulanji pakumpemphera Iye?

16. Taonani, zokoma zao siziri m'dzanja lao;(Koma uphungu wa oipa unditalikira.)

17. Ngati nyali za oipa zizimidwa kawiri kawiri?Ngati tsoka lao liwagwera?Ngati Mulungu awagawira zowawa mu mkwiyo wace?

18. Ngati akunga ziputu zomka ndi mphepo,Ngati mungu wouluzika ndi nkuntho?

19. Mukuti, Mulungu asungira ana ace a munthu coipa cace,Ambwezere munthuyo kuti acidziwe.

20. Aone yekha cionongeko cace m'maso mwace,Namwe mkwiyo wa Wamphamvuyonse.

Werengani mutu wathunthu Yobu 21