Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 20:8-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Adzauluka ngati loto, osapezekanso;Nadzaingidwa ngati masomphenya a usiku.

9. Diso lidamuonalo silidzamuonanso;Ndi malo ace sadzampenyanso.

10. Ana ace adzapempha aumphawi awakomere mtima;Ndi manja ace adzabweza cuma cace.

11. Mafupa ace adzala nao unyamata wace,Koma udzagona naye pansi m'pfumbi.

12. Cinkana coipa cizuna m'kamwa mwace,Cinkana acibisa pansi pa lilime lace;

13. Cinkana acisunga, osacileka,Naoikhalitsa m'kamwa mwace;

14. Koma cakudya cace cidzasandulika m'matumbo mwace,Cidzakhala ndulu ya mphiri mkati mwace.

15. Anacimeza cuma koma adzacisanzanso;Mulungu adzaciturutsa m'mimba mwace.

16. Adzayamwa ndulu ya mphiri;Pakamwa pa njoka padzamupha.

17. Sadzapenyerera timitsinje,Toyenda nao uci ndi mafuta.

18. Cimene adagwiriraco nchito, adzacibweza, osacimeza;Sadzakondwera monga mwa zolemera zace adaziona.

Werengani mutu wathunthu Yobu 20