5. Kuti kupfuula kokondwera kwa woipa sikukhalira kutha,Ndi cimwemwe ca wonyoza Mulungu cikhala kamphindi?
6. Cinkana ukulu wace ukwera kumka kuthambo,Nugunda pamitambo mutu wace;
7. Koma adzatayika kosatha ngati zonyansa zace;Iwo amene adamuona adzati, Ali kuti iye?
8. Adzauluka ngati loto, osapezekanso;Nadzaingidwa ngati masomphenya a usiku.
9. Diso lidamuonalo silidzamuonanso;Ndi malo ace sadzampenyanso.
10. Ana ace adzapempha aumphawi awakomere mtima;Ndi manja ace adzabweza cuma cace.
11. Mafupa ace adzala nao unyamata wace,Koma udzagona naye pansi m'pfumbi.
12. Cinkana coipa cizuna m'kamwa mwace,Cinkana acibisa pansi pa lilime lace;
13. Cinkana acisunga, osacileka,Naoikhalitsa m'kamwa mwace;
14. Koma cakudya cace cidzasandulika m'matumbo mwace,Cidzakhala ndulu ya mphiri mkati mwace.
15. Anacimeza cuma koma adzacisanzanso;Mulungu adzaciturutsa m'mimba mwace.
16. Adzayamwa ndulu ya mphiri;Pakamwa pa njoka padzamupha.
17. Sadzapenyerera timitsinje,Toyenda nao uci ndi mafuta.
18. Cimene adagwiriraco nchito, adzacibweza, osacimeza;Sadzakondwera monga mwa zolemera zace adaziona.
19. Pakuti anapsinja, nasiya aumphawi;Analanda nyumba mwaciwawa, imene sanaimanga.
20. Popeza sanadziwa kupumula m'kati mwace,Sadzalanditsa kanthu ka zofunika zace.