Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 20:18-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Cimene adagwiriraco nchito, adzacibweza, osacimeza;Sadzakondwera monga mwa zolemera zace adaziona.

19. Pakuti anapsinja, nasiya aumphawi;Analanda nyumba mwaciwawa, imene sanaimanga.

20. Popeza sanadziwa kupumula m'kati mwace,Sadzalanditsa kanthu ka zofunika zace.

21. Sikunatsalira kanthu kosadya iye,Cifukwa cace zokoma zace sizidzakhalitsa.

22. Pomkwanira kudzala kwace adzakhala m'kusauka;Dzanja la yense wobvutika lidzamgwera,

23. Poti adzaze mimba yace,Mulungu adzamponyera mkwiyo wace waukali,Nadzambvumbitsira uwu pakudya iye.

24. Adzathawa cida cacitsulo,Ndi mubvi wa uta wamkuwa udzampyoza.

Werengani mutu wathunthu Yobu 20