17. Sadzapenyerera timitsinje,Toyenda nao uci ndi mafuta.
18. Cimene adagwiriraco nchito, adzacibweza, osacimeza;Sadzakondwera monga mwa zolemera zace adaziona.
19. Pakuti anapsinja, nasiya aumphawi;Analanda nyumba mwaciwawa, imene sanaimanga.
20. Popeza sanadziwa kupumula m'kati mwace,Sadzalanditsa kanthu ka zofunika zace.
21. Sikunatsalira kanthu kosadya iye,Cifukwa cace zokoma zace sizidzakhalitsa.