15. Anacimeza cuma koma adzacisanzanso;Mulungu adzaciturutsa m'mimba mwace.
16. Adzayamwa ndulu ya mphiri;Pakamwa pa njoka padzamupha.
17. Sadzapenyerera timitsinje,Toyenda nao uci ndi mafuta.
18. Cimene adagwiriraco nchito, adzacibweza, osacimeza;Sadzakondwera monga mwa zolemera zace adaziona.
19. Pakuti anapsinja, nasiya aumphawi;Analanda nyumba mwaciwawa, imene sanaimanga.
20. Popeza sanadziwa kupumula m'kati mwace,Sadzalanditsa kanthu ka zofunika zace.
21. Sikunatsalira kanthu kosadya iye,Cifukwa cace zokoma zace sizidzakhalitsa.
22. Pomkwanira kudzala kwace adzakhala m'kusauka;Dzanja la yense wobvutika lidzamgwera,
23. Poti adzaze mimba yace,Mulungu adzamponyera mkwiyo wace waukali,Nadzambvumbitsira uwu pakudya iye.
24. Adzathawa cida cacitsulo,Ndi mubvi wa uta wamkuwa udzampyoza.