Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 19:4-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo ngati ndalakwa ndithu,Kulakwa kwanga kuli ndi ine ndekha.

5. Ngati inu mudzikuza ndithu pa ine,Ndi kundichulira mtonzo wanga kuti munditsutse nao;

6. Dziwani tsopano kuti Mulungu wandikhotetsera mlandu wanga,Nandizinga ndi ukonde wace.

7. Taonani, ndipfuula kuti, Ciwawa! koma sandimvera;Ndikuwa, koma palibe ciweruzo.

8. Iye ananditsekera njira kuti ndisapitireko,Naika mdima poyendapo ine.

9. Anandibvula ulemerero wanga,Nandicotsera korona pamutu panga,

10. Nandigamula ponsepo, ndipo ndamukatu;Nacizula ciyembekezo canga ngati mtengo.

11. Wandiyatsiranso mkwiyo wace,Nandiyesera ngati wina wa adani ace.

12. Ankhondo ace andidzera pamodzi, nandiundira njira yao,Nandimangira misasa pozinga hema wanga.

Werengani mutu wathunthu Yobu 19