Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 19:13-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Iye anandicotsera abale anga kutali,Ndi odziwana nane andiyesa mlendo konse.

14. Anansi anga andisowa,Ndi odziwana nane bwino andiiwala.

15. Iwo a m'nyumba mwanga ndi adzakazi anga andiyesa mlendo;Ndine wacilendo pamaso pao.

16. Ndikaitana kapolo wanga, sandibwezera mau,Cinkana ndimpembedza pakamwa panga.

17. Mpweya wanga unyansira mkazi wanga,Cinkana ndinampembedza ndi kuchula ana a thupi langa.

18. Angakhale ana ang'ono andipeputsa,Ndikanyamuka, andinena;

19. Mabwenzi anga eni eni onse anyansidwa nane;Ndi onse ndakondana nao asandulika adani anga.

20. Pfupa langa laumirira pa khungu langa ndi mnofu wanga,Ndipo ndapulumuka ndiri nazo nkhama za mano anga.

21. Ndicitireni cifundo, ndicitireni cifundo, mabwenzi anga inu;Pakuti dzanja la Mulungu landikhudza.

22. Mundilondola bwanji ngati Mulungu,Losakukwanirani thupi langa?

23. Ha! akadalembedwa mau anga!Ha! akadalembedwa m'buku!

24. Akadawazokota pathanthwe cikhalire,Ndi cozokotera cacitsulo ndi kuthira ntobvu!

25. Koma ndidziwa kuti Mombolo wanga ali ndi moyo,Nadzauka potsiriza papfumbi.

26. Ndipo khungu langa litaonongeka,Pamenepo wopanda thupi langa, ndidzapenya Mulungu;

Werengani mutu wathunthu Yobu 19