Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 19:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma Yobu anayankha, nati,

2. Mudzasautsa moyo wanga kufikira liti,Ndi kundityolatyola nao mau?

3. Kakumi aka mwandicititsa manyazi;Mulibe manyazi kuti mundiumira mtima.

4. Ndipo ngati ndalakwa ndithu,Kulakwa kwanga kuli ndi ine ndekha.

5. Ngati inu mudzikuza ndithu pa ine,Ndi kundichulira mtonzo wanga kuti munditsutse nao;

6. Dziwani tsopano kuti Mulungu wandikhotetsera mlandu wanga,Nandizinga ndi ukonde wace.

7. Taonani, ndipfuula kuti, Ciwawa! koma sandimvera;Ndikuwa, koma palibe ciweruzo.

8. Iye ananditsekera njira kuti ndisapitireko,Naika mdima poyendapo ine.

9. Anandibvula ulemerero wanga,Nandicotsera korona pamutu panga,

10. Nandigamula ponsepo, ndipo ndamukatu;Nacizula ciyembekezo canga ngati mtengo.

11. Wandiyatsiranso mkwiyo wace,Nandiyesera ngati wina wa adani ace.

Werengani mutu wathunthu Yobu 19