Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 18:9-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Msampha udzamgwira kucitende,Ndi khwekhwe lidzamkola.

10. Msampha woponda umbisikira pansi,Ndi msampha wa cipeto panjira.

11. Zoopetsa zidzamcititsa mantha monsemo,Nadzampitikitsa kumbuyo kwace.

12. Njala idzatha mphamvu yace,Ndi tsoka lidzamkonzekeratu pambali pace.

13. Zidzatha ziwalo za thupi lace,Mwana woyamba wa imfa adzatha ziwalo zace.

14. Adzazulidwa kuhema kwace kumene anakhulupirira;Nadzatengedwa kumka naye kwa mfumu ya zoopsa.

15. Adzakhala m'hema mwace iwo amene sali ace;Miyala yasulfure idzawazika pokhala pace.

16. Mizu yace idzauma pansi,Ndi nthambi yace idzafota m'mwamba.

Werengani mutu wathunthu Yobu 18