15. Adzakhala m'hema mwace iwo amene sali ace;Miyala yasulfure idzawazika pokhala pace.
16. Mizu yace idzauma pansi,Ndi nthambi yace idzafota m'mwamba.
17. Cikumbukilo cace cidzatayika m'dziko,Ndipo adzasowa dzina kukhwalala.
18. Adzamkankha acoke ku kuunika alowe kumdima;Adzampitikitsa acoke m'dziko lokhalamo anthu.
19. Sadzakhala naye mwana kapena cidzukulu mwa anthu amtundu wace,Kapena wina wotsalira kumene anakhalako.