19. Tsopanonso, taona, mboni yanga iri kumwamba,Ndi nkhoswe yanga ikhala m'mwamba.
20. Mabwenzi anga andinyoza; Koma diso langa lilirira misozi kwa Mulungu;
21. Ha! munthu akadapembedzera mnzace kwa Mulungu,Monga munthu apembedzera mnansi wace!
22. Pakuti zitafika zaka zowerengeka,Ndidzamuka ku njira imene sindibwererako.