Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 16:17-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Pangakhale palibe ciwawa m'manja mwanga,Ndi pemphero langa ndi loyera.

18. Dziko iwe, usakwirire mwazi wanga,Ndi kulira kwanga kusowe popumira.

19. Tsopanonso, taona, mboni yanga iri kumwamba,Ndi nkhoswe yanga ikhala m'mwamba.

20. Mabwenzi anga andinyoza; Koma diso langa lilirira misozi kwa Mulungu;

21. Ha! munthu akadapembedzera mnzace kwa Mulungu,Monga munthu apembedzera mnansi wace!

Werengani mutu wathunthu Yobu 16