Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 16:10-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Iwo anandiyasamira pakamwa pao;Anandiomba pama ndi kunditonza;Asonkhana pamodzi kunditsutsa.

11. Mulungu andipereka kwa osalungama,Nandiponya m'manja a oipa.

12. Ndinali mkupuma, koma anandityola;Inde anandigwira pakhosi, nandiphwanya;Anandiimika ndikhale candamali.

13. Eni mauta ace andizinga,Ang'amba imso zanga, osazileka;Natsanulira pansi ndulu yanga.

14. Andipasula-pasula;Andithamangira ngati wamphamvu.

15. Ndadzisokerera ciguduli ku khungu langa,Ndipo ndaipsa mphamvu yanga m'pfumbi.

16. Nkhope yanga njodetsedwa ndi kulira misozi,Ndi pa zikope zanga pali mthunzi wa imfa;

17. Pangakhale palibe ciwawa m'manja mwanga,Ndi pemphero langa ndi loyera.

18. Dziko iwe, usakwirire mwazi wanga,Ndi kulira kwanga kusowe popumira.

19. Tsopanonso, taona, mboni yanga iri kumwamba,Ndi nkhoswe yanga ikhala m'mwamba.

20. Mabwenzi anga andinyoza; Koma diso langa lilirira misozi kwa Mulungu;

21. Ha! munthu akadapembedzera mnzace kwa Mulungu,Monga munthu apembedzera mnansi wace!

Werengani mutu wathunthu Yobu 16