Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 15:31-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Asatame zopanda pace, kudzinyenga nazo;Pakuti zopanda pace zidzakhala combwezera cace.

32. Cidzacitika isanadze nthawi yace;Pakuti nthambi yace siidzaphuka.

33. Adzayoyoka zipatso zace zosapsa ngati mpesa,Nadzathothoka maluwa ace ngati mtengo wazitona.

34. Pakuti msonkhano wa onyoza Mulungu udzakhala cumba,Ndi moto udzapsereza mahema a olandira cokometsera mlandu.

35. Aima ndi cobvuta, nabala mphulupulu,Ndi m'mimba mwao mukonzeratu cinyengo.

Werengani mutu wathunthu Yobu 15