27. Popeza anakuta nkhope yace ndi kunenepa kwace,Nacita mafunyenye a mafuta m'zuuno zace;
28. Adzakhala m'midzi yopasuka,M'nyumba zosakhalamo munthu,Zoti zisandulika muunda.
29. Sadzakhala wolemera, ndi cuma cace sicidzakhalitsa,Ndi zipatso zace sizidzacuruka padziko.
30. Sadzacoka mumdima;Lawi la moto lidzaumitsa nthambi zace;Ndipo adzacoka ndi mpumo wa m'kamwa mwace.
31. Asatame zopanda pace, kudzinyenga nazo;Pakuti zopanda pace zidzakhala combwezera cace.
32. Cidzacitika isanadze nthawi yace;Pakuti nthambi yace siidzaphuka.
33. Adzayoyoka zipatso zace zosapsa ngati mpesa,Nadzathothoka maluwa ace ngati mtengo wazitona.
34. Pakuti msonkhano wa onyoza Mulungu udzakhala cumba,Ndi moto udzapsereza mahema a olandira cokometsera mlandu.
35. Aima ndi cobvuta, nabala mphulupulu,Ndi m'mimba mwao mukonzeratu cinyengo.