27. Popeza anakuta nkhope yace ndi kunenepa kwace,Nacita mafunyenye a mafuta m'zuuno zace;
28. Adzakhala m'midzi yopasuka,M'nyumba zosakhalamo munthu,Zoti zisandulika muunda.
29. Sadzakhala wolemera, ndi cuma cace sicidzakhalitsa,Ndi zipatso zace sizidzacuruka padziko.
30. Sadzacoka mumdima;Lawi la moto lidzaumitsa nthambi zace;Ndipo adzacoka ndi mpumo wa m'kamwa mwace.