Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 15:23-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ayendayenda ndi kufuna cakudya, nati, Ciri kuti?Adziwa kuti lamkonzekeratu pafupi tsiku lamdima,

24. Nsautso ndi cipsinjo zimcititsa mantha,Zimlaka ngati mfumu yokonzekeratu kunkhondo;

25. Pakuti amtambasula dzanja lace moyambana ndi Mulungu,Napikisana ndi Wamphamvuyonse.

26. Amthamangira Iye mwaliuma,Ndi zikopa zace zocindikira.

27. Popeza anakuta nkhope yace ndi kunenepa kwace,Nacita mafunyenye a mafuta m'zuuno zace;

28. Adzakhala m'midzi yopasuka,M'nyumba zosakhalamo munthu,Zoti zisandulika muunda.

29. Sadzakhala wolemera, ndi cuma cace sicidzakhalitsa,Ndi zipatso zace sizidzacuruka padziko.

30. Sadzacoka mumdima;Lawi la moto lidzaumitsa nthambi zace;Ndipo adzacoka ndi mpumo wa m'kamwa mwace.

31. Asatame zopanda pace, kudzinyenga nazo;Pakuti zopanda pace zidzakhala combwezera cace.

32. Cidzacitika isanadze nthawi yace;Pakuti nthambi yace siidzaphuka.

33. Adzayoyoka zipatso zace zosapsa ngati mpesa,Nadzathothoka maluwa ace ngati mtengo wazitona.

34. Pakuti msonkhano wa onyoza Mulungu udzakhala cumba,Ndi moto udzapsereza mahema a olandira cokometsera mlandu.

35. Aima ndi cobvuta, nabala mphulupulu,Ndi m'mimba mwao mukonzeratu cinyengo.

Werengani mutu wathunthu Yobu 15