15. Taona, Mulungu sakhulupirira opatulika ace;Ngakhale m'mwamba simuyera pamaso pace,
16. Koposa kotani nanga munthu wonyansa ndi wodetsa,Wakumwa cosalungama ngati madzi.
17. Ndidzakuonetsa, undimvere;Cimene ndinaciona, ndidzakufotokozera;
18. Cimene adacinena anzeru,Adacilandira kwa makolo ao, osacibisa;
19. Ndiwo amene analandira okha dzikoli,Wosapita mlendo pakati pao;
20. Munthu woipa adzipweteka masiku ace onse,Ndi zaka zowerengeka zisingikira woopsa.
21. M'makutu mwace mumveka zoopsetsa;Pali mtendere amfikira wakumuononga.
22. Sakhulupirira kuti adzaturukamo mumdima,Koma kuti lupanga limlindira;