Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 15:1-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha, nati,

2. Kodi mwini nzeru ayankhe ndi kudziwa kouluzika,Ndi kudzaza mimba yace ndi mphepo ya kum'mawa?

3. Kodi atsutsane ndi mnzace ndi mau akusathandiza?Kapena ndi maneno akusaphindulitsa?

4. Zedi uyesa cabe mantha,Nucepsa cilingiriro pamaso pa Mulungu.

5. Pakuti pakamwa pako paphunzitsa mphulupulu zako,Nusankha lilime la ocenjerera.

6. Pakamwa pako pakutsutsa, si ine ai.Inde milomo yako ikucitira umboni wakukutsutsa.

7. Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa?Kapena unayamba kulengedwa ndiwe, osati mapiri?

8. Kodi unamva uphungu wacinsinsi wa Mulungu?Ndipo unadzikokera nzeru kodi?

9. Udziwa ciani, osacidziwa ife?Uzindikira ciani, cosakhala mwa ife?

10. Pakati pa ife pali aimvi, ndi okalambitsa,Akuposa atate wako masiku ao,

11. Masangalatso a Mulungu akucepera kodi?Kapena uli naco cinsinsi kodi?

12. Mtima wako usonthokeranji nawe?Maso ako aphethira-phethira cifukwa ninji?

13. Kuti utembenuza mzimu wako utsutsane ndi Mulungu,Ndi kulola mau otere aturuke m'kamwa mwako.

Werengani mutu wathunthu Yobu 15