17. Mvetsetsani mau anga,Ndi kunenetsa kwanga kumveke m'makutu mwanu.
18. Taonani tsono, ndalongosola mlandu wanga;Ndidziwa kuti adzandimasula ndiri wolungama,
19. Ndaniyo adzatsutsana nane?Ndikakhala cete, ndidzapereka mzimu wanga.
20. Zinthu ziwiri zokha musandicitire,Pamenepo sindidzabisalira nkhope yanu:
21. Mundicotsere dzanja lanu kutali,Ndi kuopsa kwanu kusandicititse mantha.
22. Pamenepo muitane, ndipo ndidzayankha;Kapena ndinene ndine, ndipo mundiyankhe ndinu.
23. Mphulupulu zanga ndi zocimwa zanga ndi zingati?Mundidziwitse kulakwa kwanga ndi cimo langa,
24. Mubisiranji nkhope yanu,Ndi kundiyesa mdani wanu?