Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 13:17-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Mvetsetsani mau anga,Ndi kunenetsa kwanga kumveke m'makutu mwanu.

18. Taonani tsono, ndalongosola mlandu wanga;Ndidziwa kuti adzandimasula ndiri wolungama,

19. Ndaniyo adzatsutsana nane?Ndikakhala cete, ndidzapereka mzimu wanga.

20. Zinthu ziwiri zokha musandicitire,Pamenepo sindidzabisalira nkhope yanu:

21. Mundicotsere dzanja lanu kutali,Ndi kuopsa kwanu kusandicititse mantha.

22. Pamenepo muitane, ndipo ndidzayankha;Kapena ndinene ndine, ndipo mundiyankhe ndinu.

23. Mphulupulu zanga ndi zocimwa zanga ndi zingati?Mundidziwitse kulakwa kwanga ndi cimo langa,

24. Mubisiranji nkhope yanu,Ndi kundiyesa mdani wanu?

Werengani mutu wathunthu Yobu 13