Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 13:14-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndilumirenji mnofu wanga pamano panga,Ndi kupereka moyo wanga m'dzanja langa?

15. Angakhale andipha koma ndidzamlindira;Komanso ndidzaumirira mayendedwe anga pamaso pace.

16. Iye adzakhalanso cipulumutso canga,Pakuti wonyoza Mulungu sadzafika pamaso pace.

17. Mvetsetsani mau anga,Ndi kunenetsa kwanga kumveke m'makutu mwanu.

18. Taonani tsono, ndalongosola mlandu wanga;Ndidziwa kuti adzandimasula ndiri wolungama,

19. Ndaniyo adzatsutsana nane?Ndikakhala cete, ndidzapereka mzimu wanga.

20. Zinthu ziwiri zokha musandicitire,Pamenepo sindidzabisalira nkhope yanu:

21. Mundicotsere dzanja lanu kutali,Ndi kuopsa kwanu kusandicititse mantha.

22. Pamenepo muitane, ndipo ndidzayankha;Kapena ndinene ndine, ndipo mundiyankhe ndinu.

Werengani mutu wathunthu Yobu 13