Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 12:4-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndine ngati munthu wosekedwa ndi mnansi wace,Ndinaitana kwa Mulungu, ndipo anandiyankha;Munthu wolungama wangwiro asekedwa.

5. Munthu wosatekeseka apeputsa tsoka mumtima mwace,Limlindira woterereka mapazi ace.

6. Mahema a acifwamba akhala mumtendere,Ndi iwo oputa Mulungu alimbika mtima:Amene Mulungu amadzazira dzanja lao.

7. Tafunsira tsono kwa nyamazo, zidzakulangiza,Ndi mbalame za m'mlengalenga, zidzakuuza;

8. Kapena ulankhule ndi dziko lapansi, lidzakulangiza;Ndi nsomba za kunyanja, zidzakufotokozera,

9. Ndaniyo sadziwa nazo izi zonse;Kuti dzanja la Yehova licita ici?

10. M'dzanja mwace muli mpweya wa zamoyo zonse,Ndi mzimu wa munthu ali yense.

11. M'khutumu simuyesa mau,Monga m'kamwa mulawa cakudya cace?

12. Kwa okalamba kuli nzeru,Ndi kwa a masiku ocuruka luntha.

13. Kwa Iye kuli nzeru ndi mphamvu;Uphungu ndi luntha ali nazo.

14. Taona, agamula, ndipo palibe kumanganso;Amtsekera munthu, ndipo palibe kumtsegulira,

15. Taona atsekera madzi, naphwa;Awatsegulira, ndipo akokolola dziko lapansi.

16. Kwa Iye kuli mphamvu ndi nzeru.Wonyengedwa ndi wonyenga yemwe ali ace.

17. Apita nao maphungu atawafunkhira,Napulukiritsa oweruza milandu.

18. Amasula comangira ca mafumu,Nawamangira nsinga m'cuuno mwao.

19. Apita nao, ansembe atawafunkhica,Nagubuduza amphamvu.

20. Amcotsera wokhulupirika kunena kwace.Nalanda luntha la akulu.

21. Atsanulira mnyozo pa akalonga,Nawasezera olimba lamba lao.

22. Abvumbulutsa zozama mumdima,Naturutsa mthunzi wa imfa ukhale poyera;

23. Acurukitsa amitundu, nawaononganso;Abalalikitsa amitundu, nawabwezanso.

Werengani mutu wathunthu Yobu 12