Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 12:12-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Kwa okalamba kuli nzeru,Ndi kwa a masiku ocuruka luntha.

13. Kwa Iye kuli nzeru ndi mphamvu;Uphungu ndi luntha ali nazo.

14. Taona, agamula, ndipo palibe kumanganso;Amtsekera munthu, ndipo palibe kumtsegulira,

15. Taona atsekera madzi, naphwa;Awatsegulira, ndipo akokolola dziko lapansi.

16. Kwa Iye kuli mphamvu ndi nzeru.Wonyengedwa ndi wonyenga yemwe ali ace.

17. Apita nao maphungu atawafunkhira,Napulukiritsa oweruza milandu.

18. Amasula comangira ca mafumu,Nawamangira nsinga m'cuuno mwao.

19. Apita nao, ansembe atawafunkhica,Nagubuduza amphamvu.

Werengani mutu wathunthu Yobu 12