Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 12:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo Yobu anayankha, nati,

2. Zoonadi inu ndinu anthu,Ndi nzeru idzafa pamodzi ndi inu.

3. Koma inenso ndiri nayo nzeru monga inu.Sindingakucepereni;Ndani sadziwa zonga izi?

4. Ndine ngati munthu wosekedwa ndi mnansi wace,Ndinaitana kwa Mulungu, ndipo anandiyankha;Munthu wolungama wangwiro asekedwa.

5. Munthu wosatekeseka apeputsa tsoka mumtima mwace,Limlindira woterereka mapazi ace.

6. Mahema a acifwamba akhala mumtendere,Ndi iwo oputa Mulungu alimbika mtima:Amene Mulungu amadzazira dzanja lao.

7. Tafunsira tsono kwa nyamazo, zidzakulangiza,Ndi mbalame za m'mlengalenga, zidzakuuza;

8. Kapena ulankhule ndi dziko lapansi, lidzakulangiza;Ndi nsomba za kunyanja, zidzakufotokozera,

9. Ndaniyo sadziwa nazo izi zonse;Kuti dzanja la Yehova licita ici?

10. M'dzanja mwace muli mpweya wa zamoyo zonse,Ndi mzimu wa munthu ali yense.

Werengani mutu wathunthu Yobu 12