Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 11:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Mukakhala mphulupulu m'dzanja lako, uicotseretu kutali,Ndi cisalungamo cisakhale m'mahema mwako;

15. Popeza pamenepo udzakweza nkhope yako opanda banga;Nudzalimbika osacita mantha;

16. Pakuti udzaiwala cisoni cako,Udzacikumbukila ngati madzi opita;

17. Ndipo moyo wako udzayera koposa usana;Kungakhale kuli mdima kudzakhala ngati m'mawa.

18. Ndipo udzalimbika mtima popeza pali ciyembekezo;Nudzafunafuna, ndi kugona mosatekeseka,

19. Inde udzagona pansi, wopanda wina wakukunjenjemeretsa,Ndipo ambiri adzakupembedza,

20. Koma maso a oipa adzagoma, Ndi pothawirapo padzawasowa,Ndipo ciyembekezo cao ndico kupereka mzimu wao.

Werengani mutu wathunthu Yobu 11