Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 11:12-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Koma munthu wopanda pace asowa nzeru,Ngakhale munthu abadwa ngati mwana wa mbidzi.

13. Ukakonzeratu mtima wako,Ndi kumtambasulira Iye manja ako;

14. Mukakhala mphulupulu m'dzanja lako, uicotseretu kutali,Ndi cisalungamo cisakhale m'mahema mwako;

15. Popeza pamenepo udzakweza nkhope yako opanda banga;Nudzalimbika osacita mantha;

16. Pakuti udzaiwala cisoni cako,Udzacikumbukila ngati madzi opita;

17. Ndipo moyo wako udzayera koposa usana;Kungakhale kuli mdima kudzakhala ngati m'mawa.

18. Ndipo udzalimbika mtima popeza pali ciyembekezo;Nudzafunafuna, ndi kugona mosatekeseka,

19. Inde udzagona pansi, wopanda wina wakukunjenjemeretsa,Ndipo ambiri adzakupembedza,

Werengani mutu wathunthu Yobu 11