Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 11:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo anayankha Zofari wa ku Naama, nati,

2. Kodi mau ocurukawa sayenera kuwayankha?Ndi munthu wa milomo ayenera kuyesedwa wolungama?

3. Kodi zotamanda zako ziwatseke anthu pakamwa?Useka kodi, wopanda munthu wakukucititsapo manyazi?

4. Pakuti unena, Ciphunzitso canga ncoona,Ndipo ndiri woyera pamaso pako.

5. Koma, hal mwenzi atanena Mulungu,Ndi kukutsegulira milomo yace motsutsa;

6. Nakufotokozere zinsinsi za nzeru,Popeza zipindika-pindika macitidwe ao!Cifukwa cace dziwa kuti Mulungu akuiwalira mphulupulu zina.

7. Kodi ukhoza kupeza Mulungu mwa kufunafuna?Ukhoza kupeza Wamphamvuyonse motsindika?

Werengani mutu wathunthu Yobu 11