Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 10:8-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Manja anu anandiumba, nandiulunga monsemu,Koma mufuna kundiononga.

9. Mukumbukile kuti mwandiumba ngati dothi;Ndipo kodi mudzandibwezera kupfumbi?

10. Simunanditsanula kodi ngati mkaka,Ndi kundilimbitsa ngati mase?

11. Munandibveka khungu ndi mnofu,Ndi kundilumikiza mafupa ndi mitsempha,

12. Mwandipatsa moyo, ndi kundikomera mtima,Ndi masamalidwe anu anasunga mzimu wanga.

13. Koma izi munazibisa mumtima mwamu;Ndidziwa kuti ici muli naco:

14. Ndikacimwa mundipenya;Ndipo simudzandimasula mphulupulu yanga.

15. Ndikakhala woipa, tsoka ine;Ndikakhala wolungama, sindidzakweza mutuwanga;Ndadzazidwa ndi manyazi, Koma penyani kuzunzika kwanga.

16. Ndipo mutu wanga ukadzikweza, mundisaka ngati mkango;Mubweranso ndi kudzionetsera modabwiza kwa ine.

17. Mundikonzeranso mboni zonditsutsa,Ndi kundicurukitsira mkwiyo wanu;Nkhondo yobwereza-bwereza yandigwera.

Werengani mutu wathunthu Yobu 10