Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 10:1-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mtima wanga ulema nao moyo wanga,Ndidzadzilolera kudandaula kwanga,Ndidzalankhula pakuwawa mtima wanga.

2. Ndidzati kwa Mulungu, Musanditsutse;Mundidziwitse cifukwa ca kutsutsana nane.

3. Cikukomerani kodi kungosautsa,Kuti mupeputsa nchito yolemetsa manja anu,Ndi kuti muwalira pa uphungu wa oipa?

4. Muli nao maso a thupi kodi?Mupenya kodi monga umo apenyera munthu?

5. Masiku anu akunga masiku a munthu kodi,Zaka zanu zikunga masiku a munthu;

6. Kuti mufunsa mphulupulu yanga,Ndi kulondola coipa canga;

7. Cinkana mudziwa kuti sindiri woipa,Ndipo palibe wakupulumutsa m'dzanja lanu?

8. Manja anu anandiumba, nandiulunga monsemu,Koma mufuna kundiononga.

9. Mukumbukile kuti mwandiumba ngati dothi;Ndipo kodi mudzandibwezera kupfumbi?

10. Simunanditsanula kodi ngati mkaka,Ndi kundilimbitsa ngati mase?

11. Munandibveka khungu ndi mnofu,Ndi kundilumikiza mafupa ndi mitsempha,

12. Mwandipatsa moyo, ndi kundikomera mtima,Ndi masamalidwe anu anasunga mzimu wanga.

13. Koma izi munazibisa mumtima mwamu;Ndidziwa kuti ici muli naco:

Werengani mutu wathunthu Yobu 10