Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 10:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mtima wanga ulema nao moyo wanga,Ndidzadzilolera kudandaula kwanga,Ndidzalankhula pakuwawa mtima wanga.

2. Ndidzati kwa Mulungu, Musanditsutse;Mundidziwitse cifukwa ca kutsutsana nane.

3. Cikukomerani kodi kungosautsa,Kuti mupeputsa nchito yolemetsa manja anu,Ndi kuti muwalira pa uphungu wa oipa?

4. Muli nao maso a thupi kodi?Mupenya kodi monga umo apenyera munthu?

5. Masiku anu akunga masiku a munthu kodi,Zaka zanu zikunga masiku a munthu;

6. Kuti mufunsa mphulupulu yanga,Ndi kulondola coipa canga;

7. Cinkana mudziwa kuti sindiri woipa,Ndipo palibe wakupulumutsa m'dzanja lanu?

8. Manja anu anandiumba, nandiulunga monsemu,Koma mufuna kundiononga.

9. Mukumbukile kuti mwandiumba ngati dothi;Ndipo kodi mudzandibwezera kupfumbi?

10. Simunanditsanula kodi ngati mkaka,Ndi kundilimbitsa ngati mase?

Werengani mutu wathunthu Yobu 10