Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 1:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Koma mutambasule dzanja lanu ndi kumkhudzira zace zonse, ndipo adzakucitirani mwano pankhope panu.

12. Nati Yehova kwa Satana, Taona, zonse ali nazo zikhale m'dzanja mwako; pa iye pokha usatambasula dzanja lako. Naturuka Satana pamaso pa Yehova.

13. Tsono panali tsiku loti ana ace amuna ndi akazi analinkudya ndi kumwa vinyo m'nyumba ya mkuru wao;

14. nafika mthenga kwa Yobu, nati, Ng'ombe zinalikulima, ndi aburu akazi analikudya pambali pao;

15. koma anazigwera Aseba, nazitenga, nawapha anyamata ndi lupanga lakuthwa, ndipo ndapulumuka ine ndekha kudzakuuzani.

16. Akali cilankhulire uyu, anadza winanso, nati, Wagwa moto wa Mulungu wocokera kumwamba, wapsereza nkhosa ndi anyamata, nuzinyeketsa; ndipo ndapulumuka ine ndekha kudzakuuzani.

Werengani mutu wathunthu Yobu 1