9. Citani phokoso, anthu inu, koma mudzatyokatyoka; cherani khutu, inu nonse a maiko akutari; kwindani nokha, koma mudzatyokatyoka; kwindani nokha, koma mudzatyokatyoka.
10. Panganani upo, koma udzakhala cabe; nenani mau, koma sadzacitika; pakuti Mulungu ali pamodzi ndi ife.
11. Pakuti Yehova watero kwa ine ndi dzanja lolimba, nandilangiza ine kuti ndisayende m'njira ya anthu awa, nati,
12. Musacinene, Ciwembu; ciri conse cimene anthu awa adzacinena, Ciwembu; musaope monga kuopa kwao kapena musacite mantha.
13. Yehova wa makamu, Iye mudzamyeretsa; muope Iye, akucititseni mantha Iye.